MAFUNSO OKHUDZA ANGELO

Kodi Angelo ndi ndani? Nanga amaonekabwanji?

Iwo ndi zina mwa zolengedwa za Mulungu analengedwa kuchokera kudangalira (kuwala), Mulungu adawalenga iwo asadamulenge munthu. Iwo ali ndi chifuniro, nzeru ndi mapiko, ndipo maonekedwe a nkhope zawo ndi okongola, alinso ndikuthekera kodzisintha kuti aoneke ngati munthu, iwo samadya kapena kumwa, iwo ndi akapolo a Mulungu amapanga zomwe alamulidwa, iwo ali ndi maulemelero a pamwamba osiyanasiyana.
Ndipo wolemekezeka kwambiri mwaiwo ndi Jibir (as); iye ndi amene anapatsidwa ntchito yokafikitsa chivumbulutso (uthenga wa Mulungu) kwa atumiki.
Wina ndi Mikail;Israfil ndi ena otero, ena mwaiwo ndi amene anapatsidwa ntchito yosamalira akapolo a Mulungu nthawi ina iliyonse, ndipo pali chiwerengero chochuluka cha angelo, mngelo wina aliyense ali ndi ntchito yakeyake yomwe Mulungu anamupatsa kuti azigwira (144).

Kodi maina A Angelo ndi ati?

Ndithu angelo alipo ochuluka kwambiri, palibe amene amadziwa kuchuluka kwawo kupatula Mulungu (mwini ulemero wapamwamba), ena mwa maina awo ndi awa: Jibiril, Mikail, Israfiil, Ridhwani, Maliki (as), palinso omwe anyamula mpando wa Mulungu, ena otetezera akapolo a Mulungu, ndi ena omwe amasunga ntchito za akapolo a Mulungu, ndi ena otero (145).

Chifukwa chiyani Mulungu analenga Angelo?

Mulungu analenga angelo kuti azigwira ntchito yabwino, iwo onse ndi abwino nthawi zonse, sapanga choipa ndipo sachidziwa. Angelo kwao kweni kweni ndi kumwamba, koma kutsika kwa munthu kubwera pansi pano kunapangitsa kuti angelo ena azitsikanso pansi pano kudzagwira ntchito zawo zina zomwe Mulungu wawalamula kuti adzagwire, monga kudzawasamalira, ndikudzawatetezera ndi kuwayang’anira anthu, ndi kudzafikitsa uthenga kwa aneneri, ndikudzapulumutsa, ndikuwapemphelera chikhululuko anthu, kudzakhala nawo anthu pamalo pomwe akumutchula Mulungu ndi ntchito zina zotero.
Ndipo ndi zotheka kumuuza mwana kuti angelo ali ndi ntchito ziwiri zikulu zikulu zofunikira kwambiri izi: kupembedza Mulungu ndikuyika ndondomeko yakayendetsedwe kadziko limeneli.

Kodi nchifukwa chiyani sitimawaona Angelo?

Anthu alibe kuthekera kowaona angelo mkaonekedwe kao komwe Mulungu adawalegera. Nchifukwa chake iwo amadzisintha namaoneka ngati munthu ndicholinga choti anthu athe kuwaona iwo kapena kugwira nawo ntchito, ngati m’mene Jibiril anadzisinthila naoneka ngati munthu wachimidzi midzi pa nkhani yophunzitsa malamulo achipembedzo ija (147).

Kodi ziwanda (majini) ndi chiyani?

Izi ndizina mwa zolengedwa za Mulungu, Mulungu adazilenga izi kuchokera kumoto, ndipo iwo analengedwera kuti azimvera malamulo a Mulungu ndikusiya zomwe waletsa, iwo amamwalira ngati m’mene zolengedwa zonse zimamwalilira, ife sitingakwanitse kuziona ndipo tilibe kuthekera kotero, Mulungu adawalengera iwo kuthekera kosiyana ndi kuthekera kwa munthu, iwo amatha kuuluka ndi kuyenda mwachangu komanso amakwanitsa kudzisintha maonekedwe (kusanduka) (148), ndipo kalengedwe kawo ndikosiyana ndi kamunthu, chifukwa munthu adalengedwa kuchokera kudothi pomwe ziwanda zinalengedwa kuchokera kumoto.

Kodi wamphamvu kwambiri ndi ndani pakati pa Angelo ndi Ziwanda?

Ndithu angelo kalengedwe kawo ndikopitilira samwalira kufikira tsiku lomwe lidzaimbidwe lipenga, pomwe ziwanda zimamwalira zisanafike tsiku limeneli. Kotero angelo ndi amene amachotsa mizimu kudzera muchilolezo cha Mulungu akagamula kuti wina wake amwalire “Mulungu ndiyemwe amatenga mizimu pa nthawi ya ifa yake” (surat zumar: 42), choncho angelo ndi amphamvu kwambiri kumbali imeneyi ndi paumoyo wadziko lapansiwu, ndipo satana ndi abale ake amaopa angelo, monga m’mene zinachitikira tsiku la nkhondo ya Badri satana ataona angelo omwe Mulungu adawatumiza kuti akawathandizire anthu okhulupilira, iye anawauza makafiri kuti: “Ine ndikuzipatula mwainu, Ndithu ine ndikuona zomwe inu simukuziona, ndithu ine ndikuopa Mulungu, ndiponso Mulungu ngwaukali polanga” (surat Al Anifaal:48).

Kodi Angelo amamwalira?

Nzoona kuti angelo ndi zina mwazolengedwa za Mulungu, ndipo chilichonse chidzaoonongeka ndipo angelo adzamwalira kupatula Mulungu wapamwamba mwamba, chifukwa iye ndi wamoyo wampakana kalekale (150), Mulungu akunena kuti: “chinthu chilichonse chidzaonongeka kupatula nkhope yake (Mulunguyo)”, ( surat Al Qasas: 88), ndiye zonse zili padziko lapansi pano zidzamwalira, chimodzi modzinso zonse zomwe zili kumwamba zidzamwalira kupatula omwe Mulungu adzawafune kuti nthawi imeneyo asamwalire, ndipo palibe yemwe adzatsale osamwalira kupatula Mulungu wapamwamba mwamba, chifukwa iye ndiwamoyo yemwe sadzamwalira mpaka kale kale (wamuyaya).

Back to top button